Verse 1
Awona chilichonse nchosinthika
Mawonekedwe ulemelero wandidzadza
Wandivekanso nkhope yatsopano
Aaah aaah
Zomwe amayembekezera sizinatheke
Wawachititsa manyazi Mulungu wanga
Dzenje lomwe anakumba agweramo okha
Aaah aaah
Nsanje, kaduka, phula mmaso mwawo
Zidamata kalekale
Sangawone ubwino wanga
Kwawo ndikunyoza basi
Chorus
Pomwe mudikira kuona kugwa kwanga
Ndipomwe Mbuye akungodidalitsabe
Pomwe mudikira kuona kugwa kwanga
Ndipmwe Mbuye akungondidalitsabe
Badikiranibe
Badikiranibe
Bandikiranibe mbuye sangasiye `ndidalitsa poti mumandida inu
Verse 2
Adani anga nthawi zonse londolondo
Dobvu chuchu ngati nkango wanja
Kuti ndikangogwa andilikhwire
Aaah aaah
Koma mbuye wanga ayi sangalore
Ine ndili chete adzamenya nkhondo
Dzanja lake lamphamvu liri pa ine
Aaah aaah
Akatchera makhwekhwe, akodwamo okha
Akakumba mayenje, agweramo okha
Akapanga choipa, chimawatsata okha
Samadziwa kuti ndili ndi Yesu ineee
Chorus
Pomwe mudikira kuona kugwa kwanga
Ndipomwe Mbuye akungodidalitsabe
Pomwe mudikira kuona kugwa kwanga
Ndipomwe Mbuye akungondidalitsabe
Badikiranibe
Badikiranibe
Bandikiranibe mbuye sangasiye ndidalitsa poti mumandida inu Chorus Pomwe mudikira kuona kugwa kwanga Ndipomwe Mbuye akungodidalitsabe Pomwe mudikira kuona kugwa kwanga Ndipmwe Mbuye akungondidalitsabe Badikiranibe Badikiranibe Bandikiranibe mbuye sangasiye
ndidalitsa poti mumandida inu