Artness Ngalauka kubadwila ku Dedza m’mudzi mwa a Mfutso,kukulila ku Lilongwe ku Chilinde.Artness anabadwa pa 29 September 1983, mwana oyamba kubadwa m’banja la ana 4,akazi okhaokha.
Maitanidwe amayimbidwe anamufikila ali ndi 8 yrs pomwe a malemu Shadreck Wame anakhala naye chidwi kwambili ku Kasungu pomwe anakaimba pa msonkhano wawo ndipo miyoyo yochuluka inatembenuka mtima chifukwa Cha maimbidwe ake.Artness ali ndi zaka 10 amkapangitsa anthu ambili kubwera ku msonkhano wa 5 days wa a Shadreck Wame ku Kasungu komwe amakhala pa nthawi imeneyo.
Kuimba kunapitilila ku kwaya yomwe amaimba mu seventh day Adventist Church kufikila pomwe Artness anakula.Chidwi choyamba kuimba ngati soul artist chinakhazikika mwa iye 2008 pomwe anaganiza zotulutsa chimbale choyamba chomwe ankati Tikalowako Bwanji ndipo nyimbozi zimkaseweredwa kwambili pa Zodiac ndi Joe Mwase koma zinazangozizila chifukwa chosapanga promote nyimbozo.
Mu 2015 Artness anatulutsa chimbale china chotchedwa Ndipitabe chomwe anajambula ndi producer Anthony Makuta ndipo anthu anachilandila kwambili ndipo anachipanga launch ku South Africa mu 2018.Mu 2020 anatulutsa chimbale china chotchedwa Alipo Ondimenyera chomwe anapanganso launch ku RSA komko.2022 anatulutsa chimbale china chotchedwa Ndapanga Chisankho chomwe sanapange launch koma nyimbo zili pa website.Pano Artness akuyembekezeka kutulutsa chimbale china chomwe mutu wake ndi WAMOYO chomwe chikhale chikukhazikitsidwa mkatikati mwa 2024.Artness ali ndi dzina koma lomwe amatchuka nalo ku maimbidwe ndi HERO K.